Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 7:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Zitatha izi ndinapenya, taonani, khamu lalikuru, loti palibe munthu anakhozakuliwerenga, ocokera mwa mtundu uti wonse, ndi mafuko ndi anthu ndi manenedwe, akuimirira ku mpando wacifumu ndi pamaso pa Mwanawankhosa, atabvala zobvalazoyera, ndi makhwatha a kanjedza m'manja mwao;

10. ndipo apfuula ndi mau akuru, nanena, Cipulumutso kwa Mulungu wathu wakukhala pa mpando wacifumu, ndi kwa Mwanawankhosa.

11. Ndipo angelo onse anaimirira pozinga mpando wacifumu, ndi akulu, ndi zamoyozo zinai; ndipo anagwa nkhope yao pansi ku mpando wacifumu, nalambifa Mulungu,

12. ndi kunena, Amen: Thamo ndi ulemerero, ndi nzeru, ndi ciyamiko, ndi ulemu, ndi cilimbiko, ndi mphamvu zikhale kwa Mulungu wathu kufikira nthawi za nthawi. Amen.

13. Ndipo mmodzi wa akuru anayankha, nanena ndi ine, Iwo obvala zobvala zoyera ndiwo ayani, ndipo acokera kuti?

14. Ndipo ndinati kwa iye, Mbuye wanga, mudziwa ndinu. Ndipo anati kwaine, Iwo ndiwo akuturuka m'cisautso cacikuru; ndipo anatsuka zobvala zao, naziyeretsa m'mwazi wa Mwanawankhosa.

15. Cifukwa cace ali ku mpando wacifumu wa Mulungu; ndipo amtumikira iye usana ndi usiku m'Kacisi mwace; ndipo iye wakukhala pa mpando wacifumu adzawacitira mthunzi,

16. sadzamvanso njala, kapena ludzu, kapena, silidzawatentha dzuwa, kapena citungu ciri conse;

17. cifukwa Mwanawankhosa wakukhala pakati pa mpando wacifumu adzawaweta, nadzawatsogolera ku akasupe a madzi a moyo, ndipo Mulungu adzawapukutira misozi yonse pamaso pao.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 7