Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 8:10-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Yoswa analawira mamawa, nayesa anthu, nakwera, iye ndi akuru a Israyeli, pamaso pa anthu a ku Ai.

11. Ndi anthu onse a nkhondo okhala naye anakwera, nayandikira nafika pamaso pa mudzi, namanga misasa kumpoto kwa Ai; koma pakati pa iye ndi Ai panali cigwa.

12. Ndipo anatenga amuna ngati zikwi zisanu, nawaika m'molalira pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa mudzi.

13. Momwemo anaika anthu, khamu lonse lokhala kumpoto kwa mudzi, ndi olalira ao kumadzulo kwa mudzi, ndipo usiku uja Yoswa analowa pakati pa cigwa,

14. Ndipo kunali, pamene mfumu ya ku Ai anaciona, anafulumira iwo, nalawira mamawa, naturuka amuna a m'mudzi kuthirana ndi Israyeli, iye ndi anthu ace onse, poikidwiratu patsogolo pa cidikha; popeza sanadziwa kuti amlalira kukhonde kwa mudzi.

15. Ndipo Yoswa ndi Aisrayeli onse anaoneka ngati a ku Ai alikuwathyola, nathawira njira ya kucipululu.

16. Pamenepo anthu onse okhala m'mudzi, anaitanidwa awapitikitse, nampitikitsa Yoswa, nakokedwa kusiyana ndi mudzi.

17. Ndipo sanatsala mwamuna mmodzi yense m'Ai kapena m'Beteli osaturukira kwa Israyeli; nasiya mudzi wapululu, napitikitsa Israyeli.

18. Pamenepo Yehova anati kwa Yoswa, Tambasula nthungo iri m'dzanja lako iloze ku Ai, pakuti ndidzaupereka m'dzanja lako. Ndipo Yoswa anatambasula nthungoyo inali m'dzanja lace kuloza mudzi.

19. Nauka msanga olalirawo m'mbuto mwao, nathamanga pamene anatambasula dzanja lace, nalowa m'mudzi, naugwira; nafulumira nayatsa mudziwo.

20. Pamene amuna a ku Ai anaceuka, anapenya, ndipo taonani, utsi wa mudzi unakwera kumwamba; nasowa mphamvu iwo kuthawa cakuno kapena cauko; ndi anthu othawira kucipululu anatembenukira owapitikitsa.

21. Ndipo pakupenya Yoswa ndi Israyeli yense kuti olalirawo adagwira mudzi, ndi kuti utsi wa mudzi unakwera, anabwerera, nawapha amuna a ku Ai.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 8