Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 13:7-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo tsopano uwagawire mapfuko asanu ndi anai, ndi pfuko la Manase logawika pakati, dziko ili likhale colowa cao.

8. Pamodzi ndi iye Arubeni ndi Agadi analandira colowa cao, cimene Mose adawapatsa tsidya ilo la Yordano kum'mawa, monga Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa;

9. kuyambira pa Aroeri, wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uti pakati pa cigwa, ndi cidikha conse ca Medeba mpaka ku Diboni;

10. ndi midzi yonse ya Sihoni mfumu ya Aamori, wakucita ufumu m'Hesiboni, mpaka malire a ana a Amoni;

11. ndi Gileadi, ndi malire a Agesuri, ndi Amaakati, ndi phiri lonse la Herimoni, ndi Basana ionse mpaka ku Saleka;

12. ufumu wonse wa Ogi m'Basana, wakucita ufumu m'Asitarotu, ndi m'Edrei (yemweyo anatsala pa otsala a Arefai); pakuti Mose anakantha awa, nawainga.

13. Koma ana a Israyeli sanainga Agesuri kapena Amaakati; koma Gesuri, ndi Maakati amakhala pakati pa Israyeli, mpaka lero lino.

14. Koma pfuko la Levi sanalipatsa colowa; nsembe za Yehova Mulungu wa Israyeli, zocitika ndi moto, ndizo colowa cace, monga iye adanena naye.

15. Ndipo Mose anapatsira pfuko la ana a Rubeni monga mwa mabanja ao.

16. Malire ao anayambira ku Aroeri wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa cigwa ndi cidikha conse ca ku Medeba;

17. Hesiboni ndi midzi yace yonse yokhala pacidikha; Diboni, ndi Bamoto-baala ndi Betibaala-Meoni;

18. ndi Yahaza ndi Kedemotu, ndi Mefaata;

19. ndi Kinyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kucigwa;

20. ndi Beti-peori, ndi matsikiro a Pisiga, ndi Beti-yesimotu;

21. ndi midzi yonse ya kucidikha, ndi ufumu wonse wa Sihoni mfumu ya Aamori, wocita ufumu m'Hesiboni, amene Mose anamkantha pamodzi ndi akalonga a Midyani, Evi, ndi Rekemu, ndi Zuri, ndi Huri ndi Reba, akalonga a Sihoni, nzika za m'dziko.

22. Ana a Israyeli anaphanso ndi lupanga Balamu mwana wa Beori, mlauli uja, pamodzi ndi ena adawaphawo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 13