Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 11:10-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Yoswa anabwerera m'mbuyo nthawi imeneyi nalanda Hazori nakantha mfumu yace ndi lupanga; pakuti kale Hazori unali waukuru wa maufumu aja onse.

11. Ndipo anakantha amoyo onse anali m'mwemo, ndi lupanga lakuthwa, ndi kuwaononga konse, osasiyapo ndi mmodzi yense wakupuma mpweya; ndipo anatentha Hazori ndi moto.

12. Ndipo Yoswa analanda midzi yonse ya mafumu awa, ndi mafumu ao omwe nawakantha ndi lupanga lakuthwa, nawaononga konse; monga Mose mtumiki wa Yehova adalamulira.

13. Koma midzi yonse yomangidwa pa zitunda zao Israyeli sanaitentha, koma wa Hazori wokha; wnenewu Yoswa anautentha.

14. Ndi zofunkha zonse za midzi iyi ndi ng'ombe ana a Israyeli anadzifunkhira; koma anakantha ndi lupanga lakuthwa anthu onse mpaka adawaononga osasiyapo ndi mmodzi yense wopuma mpweya.

15. Monga Yehova adalamulira Mose mtumiki wace, momwemo Mose analamulira Yoswa; momwemonso anacita Yoswa; sanacotsapo mau amodzi pa zonse Yehova adalamulira Mose.

16. Motero Yoswa analanda dziko lonselo, la kumapiri, ndi la kumwera, ndi dziko lonse la Goseni, ndi dziko la kucidikha, ndi la kucigwa; ndi la kwnapiri la Israyeli, ndi la ku cidikha cace;

17. kuyambira phiri la Halaki lokwera kumka ku Seiri, mpaka Baala-gadi m'cigwa ca Lebano patsinde pa phiri la Herimoni; nagwira mafwnu ao onse, nawakantha, nawapha.

18. Yoswa anathira nkhondo mafwnu awa onse nthawi yaikuru.

19. Palibe mudzi wakupangana mtendere ndi ana a Israyeli, koma Ahivi okhala m'Gibeoni; anaigwira yonse ndi nkhondo.

20. Pakuti cidadzera kwa Yehova kulimbitsa mitima yao kuti athirane nao Aisrayeli nkhondo kuti iye awaononge konse, kuti asawacitire cifundo koma awaononge, monga Yehova adalamulira Mose.

21. Ndipo Yoswa anadza nthawi yomweyo, napasula Aanaki kuwacotsa kumapiri, ku Hebroni, ku Dibiri, ku Anabi, ndi ku mapiri onse a Yuda, ndi ku mapiri onse a Israyeli; Yoswa anawaononga konse, ndi midzi yao yomwe.

22. Panalibe Aanaki otsala m'dziko la ana a Israyeli; koma m'Gaza, ndi m'Gati ndi m'Asidodo anatsalamo ena.

23. Motero Yoswa analanda dziko lonse monga mwa zonse Yehova adazinena kwa Mose; ndipo Yoswa analipereka kwa Israyeli, likhale lao lao, pfuko liri lonse gawo lace. Ndipo dziko linapumula nkhondo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 11