Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 10:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Pamenepo Yoswa ananena nao, Musaope, musatenge nkhawa; khalani amphamvu, nimulimbike mtima; pakuti Yehova adzatero ndi adani: anu onse amene mugwirana nao: nkhondo.

26. Ndipo atatero, Yoswa anawakantha nawapha, nawapacika pa mitengo isanu; nalikupacikidwa pa mitengo mpaka madzulo.

27. Ndipo kunali, nthawi yakulowa dzuwa, Yoswa analamulira kuti awatsitse kumitengo; ndipo anawataya m'phanga m'mene adabisala; naika miyala yaikuru pakamwa pa phanga, mpaka lero lomwe lino.

28. Ndipo Yoswa anagwira Makeda tsiku lomwe lija ndi kuukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi mfumu yace yom we; anawaononga konse, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyapo ndi mmodzi yense, nacitira mfumu ya ku Makeda monga anacitira mfumu ya ku Yeriko.

29. Pamenepo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye anapitirira kucokera ku Makeda kumka ku Libina, nathira nkhondo pa Libina;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 10