Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 66:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atero Yehova, Kumwamba ndi mpando wanga wacifumu, ndi dziko lapansi ndi coikapo mapazi anga; mudzandimangira Ine nyumba yotani? ndi malo ondiyenera kupumamo ali kuti?

2. Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.

3. Wakupha ng'ombe alingana ndi wakupha munthu; iye wapereka nsembe ya mwana wa nkhosa alingana ndi wotyola khosi la garu; wothira nsembe yaufa akunga wothira mwazi wa nkhumba; wofukiza conunkhira akunga wodalitsa fano; inde iwo asankha njira zao zao, ndipo moyo wao ukondwerera m'zonyansa zao;

4. Inenso ndidzasankha zodzinyenga nazo, ndipo ndidzatengera mantha ao pa iwo; pakuti pamene ndinaitana, panalibe woyankha; pamene ndinalankhula, iwo sanamva konse; koma anacita coipa m'maso mwanga, ndi kusankha cimene ndisanakondwere naco.

5. Imvani mau a Yehova, inu amene munthunthumira ndi mau ace; abale anu amene akudani inu, amene anaponya inu kunja cifukwa ca dzina langa, iwo anati, Yehova alemekezedwe, kuti ife tione kusangalala kwanu; koma iwo adzakhala ndi manyazi.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 66