Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 62:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo amitundu adzaona cilungamo cako, ndi mafumu onse ulemerero wako; ndipo udzachedwa dzina latsopano, limene m'kamwa mwa Yehova mudzachula.

3. Iwe udzakhalanso korona wokongola m'dzanja la Yehova, korona wacifumu m'dzanja la Mulungu wako.

4. Iwe sudzachedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzachedwanso Bwinja; koma iwe udzachedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.

5. Pakuti monga mnyamata akwatira namwali, momwemo ana ako amuna adzakukwama iwe; ndi monga mkwati akondwera ndi mkwatibwi, momwemo Mulungu wako adzakondwera nawe.

6. Ndaika alonda pa malinga ako, Yerusalemu; iwo sadzakhala cete usana pena usiku; inu akukumbutsa Yehova musakhale cete,

7. ndipo musamlole akhale cete, kufikira Iye atakhazikitsa naika Yerusalemu akhale tamando m'dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 62