Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 44:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Yimbani m'mwamba inu, pakuti Yehova wacicita ico; kuwani inu, mbali za pansi pa dziko; yimbani mapiri inu; nkhalango iwe, ndi mitengo yonse m'menemo; cifukwa kuti Yehova wapulumutsa Yakobo, ndipo adzadzilemekezetsa yekha mwa Israyeli.

24. Atero Yehova, Mombolo wako, ndi Iye amene anakuumba iwe m'mimba, Ine ndine Yehova, amene ndipanga zinthu zonse, ndi kufunyulula ndekha zakumwamba, ndi kuyala dziko lopansi; ndani ali ndi Ine?

25. Ndine amene nditsutsa zizindikilo za matukutuku, ndi kucititsa misala oombeza ula; ndi kubwezera m'mbuyo anthu anzeru, ndi kupusitsa nzeru zao:

26. Ndine amene ndilimbitsa mau a mtumiki wanga, kucita uphungu wa amithenga anga; ndi kunena za Yerusalemu, Adzakhalamo anthu; ndi za midzi ya Yuda; Idzamangidwa; ndipo ndidzautsa malo abwinja ace.

27. Ndine amene nditi kwa nyanja yakuya, Iphwa, ndipo ndidzaumitsa nyanja zako;

28. ndi kunena za Koresi, Iye ndiye mbusa wanga, ndipo adzacita zofuna zanga zonse; ndi kunena za Yerusalemu, Adzamangidwa; ndi kwa Kacisi, Maziko ako adzaikidwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 44