Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 49:20-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Cifukwa cace tamvani uphungu wa Yehova, umene waupangira pa Edomu; ndi zimene walingalirira okhala m'Temani, ndithu adzawakoka, ana ang'ono a zoweta; ndithu adzayesa busa lao bwinja pamodzi nao.

21. Dziko lapansi linthunthumira ndi phokoso Ija kugwa kwao; pali mpfuu, phokoso lace limveka pa Nyanja Yofiira.

22. Taonani, adzafika nadzauluka ngati ciombankhanga, adzatambasulira Boma mapiko ace, ndipo tsiku lomwelo mtima wa anthu amphamvu a Edomu adzakhala ngati mtima wa mkazi alinkudwala.

23. Za Damasiko. Hamati ndi Aripadi ali ndi manyazi, cifukwa anamva malodza, asungunuka kunyanja, adera nkhawa osatha kukhala cete.

24. Damasiko walefuka, atembenukira kuti athawe, kunthunthumira kwamgwira; zobvuta ndi kulira zamgwira iye, ngati mkazi alimkudwala.

25. Alekeranji kusiya mudzi wa cilemekezo, mudzi wa cikondwero canga?

26. Cifukwa cace anyamata ace adzagwa m'miseu yace, ndipo anthu onse a nkhondo adzatontholetsedwa tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu.

27. Ndipo Ine ndidzayatsa moto m'khoma la Damasiko, udzathetsa zinyumba za Beni-Hadadi.

28. Za Kedara, ndi za maufumu a Hazori, amene anawakantha Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo.Yehova atero: Ukani, kwerani ku Kedara, funkhani ana a kum'mawa.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 49