8. Aneneri amene analipo kale ndisanakhale ine, nimusanakhale inu, ananenera maiko ambiri, ndi maufumu akuru, za nkhondo, ndi za coipa, ndi za caola.
9. Mneneri amene anenera za mtendere, pamene mau a mneneri adzacitidwa, pamenepo mneneri adzadziwika, kuti Yehova anamtuma ndithu.
10. Pamenepo Hananiya anacotsa gori pa khosi la Yeremiya, nalityola.
11. Ndipo Hananiya ananena pamaso pa anthu onse, kuti, Yehova atero: Comweco ndidzatyola gori la Nebukadinezara mfumu ya Babulo zisanapite zaka ziwiri zamphumphu kulicotsa pa khosi la amitundu onse. Ndipo Yeremiya mneneri anacoka.
12. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yeremiya, atatyola Hananiya mneneri gori kulicotsa pa khosi la Yeremiya, kuti,
13. Pita, nunene kwa Hananiya, kuti Yehova atero: Watyola magori amtengo; koma udzapanga m'malo mwao magori acitsulo.
14. Pakuti atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Ndaika gori lacitsulo pa khosi la amitundu onsewa, kuti amtumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo; ndipo adzamtumikira iye; ndipo ndampatsanso nyama za kuthengo.
15. Ndipo Yeremiya mneneri ananena kwa Hananiya mneneri, Tamvatu, Hananiya; Yehova sanakutuma iwe; koma ukhulupiritsa anthu awa zonama.
16. Cifukwa cace Yehova atero, Taona, Ine ndidzakucotsa iwe kudziko; caka cino udzafa, pakuti wanena zopikisana ndi Yehova.
17. Ndipo anafa Hananiya caka comweco mwezi wacisanu ndi ciwiri.