Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 25:5-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ndi kuti, Mubwerere tsopano nonsenu, yense kuleka njira yace yoipa, ndi zoipa za nchito zanu, ndi kukhala m'dziko limene Yehova anapatsa inu ndi makolo anu, kuyambira kale kufikira muyaya;

6. musatsate milungu yina kuitumikira, ndi kuigwadira, musautse mkwiyo wanga ndi nchito ya manja anu; ndingacitire inu coipa.

7. Koma simunandimvera Ine, ati Yehova; kuti muutse mkwiyo wanga ndi nchito ya manja anu ndi kuonapo coipa inu.

8. Cifukwa cace Yehova wa makamu atero: Popeza simunamvera mau anga,

9. taonani, Ine ndidzatuma ndi kutenga mabanja onse a kumpoto, ati Yehova, ndipo ndidzatuma kwa Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo, mtumiki wanga, ndipo ndidzatengera iwo pa dziko lino, ndi pa okhalamo ace onse, ndi pa mitundu iyi yozungulira, ndipo ndidzathetsa iwo ndithu, ndi kuwayesa iwo cizizwitso, ndi cotsonyetsa, ndi bwinja lamuyaya.

10. Ndiponso ndidzawacotsera mau akusekera ndi mau akukondwera, ndi mau a mkwati, ndi mau a mkwatibwi, mau a mphero, ndi kuwala kwa nyali.

11. Ndipo dziko lonseli lidzakhala labwinja, ndi cizizwitso, ndipo mitundu iyi idzatumikira mfumu ya ku Babulo zaka makumi asanu ndi awiri.

12. Ndipo kudzakhala, zitapita zaka makumi asanu ndi awiri, ndzidzalanga mfumu ya ku Babulo, ndi mtundu uja womwe, ati Yehova, cifukwa ca mphulupulu zao, ndi dziko la Akasidi; ndipo ndidzaliyesa mabwinja amuyaya.

13. Ndipo ndidzatengera dzikolo mau anga onse amene ndinanenera ilo, mau onse olembedwa m'buku ili, amene Yeremiya wanenera mitundu yonse.

14. Pakuti mitundu yambiri ndi mafumu akuru adzayesa iwo atumiki ao; ndipo ndidzabwezera iwo monga mwa macitidwe ao, monga mwa nchito ya manja ao.

15. Pakuti Yehova, Mulungu wa Israyeli, atero kwa ine, Tenga cikho ca vinyo wa ukaliwu pa dzanja langa, ndi kumwetsa mitundu yonse, imene ndikutumizirako.

16. Ndipo adzamwa, nadzayenda dzandi dzandi, nadzacita misala, cifukwa ca lupanga limene Ine ndidzatumiza mwa iwo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 25