Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 24:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova anandionetsa ine, ndipo, taonani, mitanga iwiri ya nkhuyu yoikidwa pakhomo pa Kacisi wa Yehova; Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo atacotsa am'nsinga Yekoniya mwana wace wa Yehoyakimu, mfumu ya Yuda, ndi akuru a Yuda, ndi amisiri ndi acipala, kuwacotsa ku Yerusalemu, nawatengera ku Babulo.

2. Mtanga umodzi unali ndi nkhuyu zabwinobwino, ngati nkhuyu zoyamba kuca; ndipo mtanga umodzi unali ndi nkhuyu zoipaipa, zosadyeka, zinali zoipa.

3. Ndipo Yehova anati kwa ine, Kodi uona ciani, Yeremiya? Ndipo ndinati, Nkhuyu, nkhuyu zabwino, nzabwino ndithu; zoipazo nzoipa ndithu, zosadyeka poti nzoipa.

4. Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,

5. Cifukwa Yehova, Mulungu wa Israyeli, atero, Monga nkhuyu zabwino izi, momwemo ndidzasamalira am'nsinga a Yuda, amene ndawacotsera m'malo muno kunka ku dziko la Akasidi, kuwacitira bwino.

6. Pakuti ndidzaika maso anga pa iwo kuti ndiwacitire iwo bwino, ndipo ndidzawabwezanso ku dziko ili: ndipo ndidzamangitsa mudzi wao, osawapasula; ndi kuwabzyala, osawazula iwo.

7. Ndipo ndidzapatsa iwo mtima wakundidziwa, kuti ndine Yehova; nadzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wao; pakuti adzabwera kwa Ine ndi mtima wao.

8. Ndipo, monga nkhuyu zoipa, zosadyeka, poti nzoipa; ntheradi atero Yehova, Comweco ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda, ndi akulu ace, ndi otsala a m'Yerusalemu, amene atsala m'dziko ili, ndi amene akhala m'dziko la Aigupto.

9. Ndipo ndidzawapatsa akhale coopsetsa coipa ku maufumu a dziko lapansi; akhale citonzo ndi nkhani ndi coseketsa, ndi citemberero, monse m'mene ndidzawapitikitsiramo.

10. Ndipo ndidzatuma lupanga, ndi njala, ndi caola mwa iwo, mpaka athedwa m'dziko limene ndinapatsa iwo ndi makolo ao.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 24