Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42
  43. 43
  44. 44
  45. 45
  46. 46
  47. 47
  48. 48
  49. 49
  50. 50
  51. 51
  52. 52

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Za mitanga iwiri ya nkhuyu; za mtundu wao m'tsogolo

1. Yehova anandionetsa ine, ndipo, taonani, mitanga iwiri ya nkhuyu yoikidwa pakhomo pa Kacisi wa Yehova; Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo atacotsa am'nsinga Yekoniya mwana wace wa Yehoyakimu, mfumu ya Yuda, ndi akuru a Yuda, ndi amisiri ndi acipala, kuwacotsa ku Yerusalemu, nawatengera ku Babulo.

2. Mtanga umodzi unali ndi nkhuyu zabwinobwino, ngati nkhuyu zoyamba kuca; ndipo mtanga umodzi unali ndi nkhuyu zoipaipa, zosadyeka, zinali zoipa.

3. Ndipo Yehova anati kwa ine, Kodi uona ciani, Yeremiya? Ndipo ndinati, Nkhuyu, nkhuyu zabwino, nzabwino ndithu; zoipazo nzoipa ndithu, zosadyeka poti nzoipa.

4. Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,

5. Cifukwa Yehova, Mulungu wa Israyeli, atero, Monga nkhuyu zabwino izi, momwemo ndidzasamalira am'nsinga a Yuda, amene ndawacotsera m'malo muno kunka ku dziko la Akasidi, kuwacitira bwino.

6. Pakuti ndidzaika maso anga pa iwo kuti ndiwacitire iwo bwino, ndipo ndidzawabwezanso ku dziko ili: ndipo ndidzamangitsa mudzi wao, osawapasula; ndi kuwabzyala, osawazula iwo.

7. Ndipo ndidzapatsa iwo mtima wakundidziwa, kuti ndine Yehova; nadzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wao; pakuti adzabwera kwa Ine ndi mtima wao.

8. Ndipo, monga nkhuyu zoipa, zosadyeka, poti nzoipa; ntheradi atero Yehova, Comweco ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda, ndi akulu ace, ndi otsala a m'Yerusalemu, amene atsala m'dziko ili, ndi amene akhala m'dziko la Aigupto.

9. Ndipo ndidzawapatsa akhale coopsetsa coipa ku maufumu a dziko lapansi; akhale citonzo ndi nkhani ndi coseketsa, ndi citemberero, monse m'mene ndidzawapitikitsiramo.

10. Ndipo ndidzatuma lupanga, ndi njala, ndi caola mwa iwo, mpaka athedwa m'dziko limene ndinapatsa iwo ndi makolo ao.