Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:28-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo Mose anati, Ndi ici mudzadziwa kuti Yehova wanditumiza ine kucita nchito izi zonse, ndi kuti sizifuma m'mtima mwanga mwanga.

29. Akafa anthu awa monga amafa anthu onse, kapena akasungika monga amasungika anthu onse, Yehova sananditumiza ine.

30. Koma Yehova akalenga cinthu catsopano, ndi nthaka ikayasama pakamwa pace, nikawameza ndi zonse ali nazo, nakatsikira iwo kumanda ali ndi moyo; pamenepo mudzadziwa kuti anthu awa anyoza Mulungu.

31. Ndipo kunali, pakutha iye kunena mau awa onse, nthaka inang'ambika pansi pao;

32. ndi dziko linayasama pakamwa pace ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.

33. Comweco iwowa, ndi onse anali nao, anatsikira kumanda ali ndi moyo, ndi dziko linasunama pa iwo, ndipo anaonongeka pakati pa msonkhano.

34. Ndipo Aisrayeli onse akukhala pozinga pao anathawa pakumva kupfuula kwao; pakuti anati, Lingatimeze dziko ifenso.

35. Ndipo mota unaturuka kwa Yehova, ndi kunyeketsa amuna mazana awiri ndi makumi asanu aja akubwera naco cofukiza.

36. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

37. Nena ndi Eleazara mwana wa Aroni wansembe, kuti aphule mbale zofukiza pakati pa moto, nutaye makalawo uko kutali; pakuti ziri zopatulika;

38. mbale zofukizazo za iwo amene adacimwira moyo wao wao, ndipo azisule zaphanthiphanthi, zikhale cibvundikilo ca guwa la nsembe; popeza anabwera nazo pamaso pa Yehova, cifukwa cace zikhala zopatulika; ndipo zidzakhala cizindikilo kwa ana a Israyeli.

39. Ndipo Eleazara wansembe anatenga mbale zofukiza zamkuwa, zimene anthu opsererawo adabwera nazo; ndipo anazisula zaphanthiphanthi zikhale cibvundikilo ca guwala nsembe;

40. cikhale cikumbutso kwa ana a Israyeli, kuti mlendo, wosati wa mbeu ya Aroni, asasendere kucita cofukiza pamaso pa Yehova; angakhale monga Kora ndi khamu lace; monga Yehova adanena naye ndi dzanja la Mose.

41. Koma m'mawa mwace khamu lonse la ana a Israyeli anadandaula pa Mose ndi Aroni, nati, Mwapha anthu a Yehova, inu.

42. Ndipo kunali, posonkhanidwa khamulo kutsutsana nao Mose ndi Aroni, kuti anaceukira cihema cokomanako; taonani, mtambo unaciphimba, ndi ulemerero wa Yehova unaoneka.

43. Ndipo Mose ndi Aroni anadza kukhomo kwa cihema cokomanako.

44. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

45. Kwerani kucoka pakati pa khamu lino, kuti ndiwathe m'kamphindi. Pamenepo adagwa nkhope zao pansi.

46. Ndipo Mose anati kwa Aroni, Tenga mbale yako yofukiza, nuikemo mota wa ku guwa la nsembe, nuikepo cofukiza, nufulumire kumuka ku khamulo, nuwacitire cowatetezera; pakuti waturuka mkwiyo pamaso pa Yehova; wayamba mliri.

Werengani mutu wathunthu Numeri 16