Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 9:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ngakhale apa atadzipangira mwana wa ng'ombe woyenga, nati, Suyu Mulungu wako anakukweza kucokera ku Aigupto, nacita zopeputsa zazikuru;

19. koma Inu mwa nsoni zanu zazikuru simunawasiya m'cipululu; mtambo woti njo sunawacokera usana kuwatsogolera m'njira, ngakhale moto wa tolo usiku kuwaunikira panjira anayenera kuyendamo.

20. Munawapatsanso mzimu wanu wokoma kuwalangiza, ndipo simunawamana mana anu pakamwa pao; munawapatsanso madzi pa ludzu lao.

21. Ndipo munawalera zaka makumi anai m'cipululu, osasowa kanthu iwo; zobvala zao sizinatha, ndi mapazi ao sanatupa.

22. Munawapatsanso maufumu, ndi mitundu ya anthu, nimunawagawa m'madera, motero analandira likhale lao lao dziko la Sihoni, ndilo dziko la mfumu ya ku Hesiboni, ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basana.

23. Ana aonso munawacurukitsa monga nyenyezi za m'mwamba, nimunawalowetsa m'dziko mudalinena kwa makolo ao, alowemo likhale lao lao.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 9