Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 9:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Koma iwo ndi makolo athu anacita modzikuza, naumitsa khosi lao, osamvera malamulo anu,

17. nakana kumvera, osakumbukilansozodabwiza zanu munazicita pakati pao; koma anaumitsa khosi lao, ndipo m'kupanduka kwao anaika mtsogoleri abwerere kumka ku ukapolo wao; koma Inu ndinu Mulungu wokhululukira, wacisomo, ndi wansoni, wolekereza, ndi wocuruka cifundo; ndipo simunawasiya.

18. Ngakhale apa atadzipangira mwana wa ng'ombe woyenga, nati, Suyu Mulungu wako anakukweza kucokera ku Aigupto, nacita zopeputsa zazikuru;

19. koma Inu mwa nsoni zanu zazikuru simunawasiya m'cipululu; mtambo woti njo sunawacokera usana kuwatsogolera m'njira, ngakhale moto wa tolo usiku kuwaunikira panjira anayenera kuyendamo.

20. Munawapatsanso mzimu wanu wokoma kuwalangiza, ndipo simunawamana mana anu pakamwa pao; munawapatsanso madzi pa ludzu lao.

21. Ndipo munawalera zaka makumi anai m'cipululu, osasowa kanthu iwo; zobvala zao sizinatha, ndi mapazi ao sanatupa.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 9