Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 3:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Eliasibu mkuru wa ansembe ananyamuka pamodzi ndi abale ace ansembe, namanga cipata cankhosa; anacipatula, naika zitseko zace, inde anacipatula mpaka nsanja ya Mea, mpaka nsanja ya Hananeeli.

2. Ndi pambali pace anamanga amuna a ku Yeriko. Ndi pambali pao anamanga Zakuri mwana wa Imri.

3. Ndi cipata cansomba anacimanga ana a Hasenaa; anamanga mitanda yace, ndi kuika zitseko zace, zokowera zace, ndi mipingiridzo yace.

4. Ndi pambali pao anakonza Meremoti mwana wa Uliya, mwana wa Kozi. Ndi pambali pao anakonza Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabele. Ndi pambali pao anakonza Zadoki mwana wa Baana.

5. Ndi pambali pao anakonza Atekoa; koma omveka ao sanapereka makosi ao ku nchito ya Mbuye wao.

6. Ndi cipata cakale anacikonza Yoyada mwana wa Paseya; ndi Mesulamu mwana wa Besodeya anamanga mitanda yace, ndi kuika zitseko zace, ndi zokowera zace, ndi mipingiridzo yace.

7. Ndi pambali pao anakonza Melatiya Mgibeoni, ndi Yadoni Mheronoti, ndi amuna a ku Gibeoni, ndi a ku Mizipa, wa ulamuliro wa ciwanga tsidya lino la mtsinje.

8. Pambali pace anakonza Uziyeli mwana wa Haraya, wa iwo osula golidi. Ndi padzanja pace anakonza Hananiya, wa iwo osanganiza zonunkhira; nalimbikitsa Yerusalemu mpaka linga lacitando.

9. Ndi pambali pao anakonza Refaya mwana wa Huri, ndiye mkuru wa dera lina la dziko la Yerusalemu.

10. Ndi pambali pao anakonza Yedaya mwana wa Harumafi, pandunji pa nyumba yace. Ndi pambali pace anakonza Hatusi mwana wa Hasabineya.

11. Malikiya mwana wa Harimu, ndi Hasubi mwana wa Pahati-Moabu, anakonzal gawo lina, ndi nsanja ya ng'anjo.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 3