Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 13:13-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndinaikanso osunga cuma, asunge nyumba za cuma: Selemiya wansembe, ndi Zadoki mlembi; ndi wa Alevi, Pedaya; ndi wakuwathandiza, Hanani mwana wa Zakuri, mwana wa Mataniya; popeza anayesedwa okhulupirika ndi udindo wao, ndiwo kugawira abale ao.

14. Mundikumbukile Mulungu wanga mwa ici, nimusafafanize zokoma zanga ndinazicitira nyumba ya Mulungu wanga, ndi maudikiro ace.

15. Masiku awa ndinaona ku Yuda ena akuponda mphesa m'coponderamo dzuwa la Sabata, ndi akubwera nayo mitolo ya tirigu, ndi kuisenzetsa pa aburu; momwemonso vinyo, mphesa, ndi nkhuyu, ndi zosenza ziri zonse, zimene analowa nazo m'Yerusalemu dzuwa la Sabata, ndipo ndinawacitira umboni wakuwatsutsa tsikuti anagulitsa zakudya.

16. Anakhalanso m'menemo a ku Turo, obwera nazo nsomba, ndi malonda ali onse, nagulitsa dzuwa la Sabata kwa ana a Yuda ndi m'Yerusalemu.

17. Pamenepo ndinatsutsana nao aufulu a Yuda, ndinanena nao, Cinthu canji coipa ici mucicita, ndi kuipsa naco dzuwa la Sabata?

18. Sanatero kodi makolo anu, ndipo Mulungu wathu anatifikitsira ife ndi mudzi uno coipa ici conse? koma inu muonjezera Israyeli mkwiyo pakuipsa Sabata.

19. Ndipo kunali, kukadayamba cizirezire pa zipata za Yerusalemu, losafika Sabata, ndinawauza atseke pamakomo; ndinawauzanso kuti asatsegulepo, koma litapita Sabata ndipo; ndipo ndinaimika anyamata anga ena pazipata, kuti pasalowe katundu dzuwa la Sabata.

20. Momwemo eni malonda ndi ogulitsa malonda ali onse, anagona kunja kwa Yerusalemu kamodzi kapena kawiri.

21. Koma ndinawacima umboni wakuwatsutsa, ndinanena nao, Mugoneranji pafupi pa linga? mukateronso ndikuthirani manja. Kuyambira pomwepo sanafikanso pa Sabata.

22. Ndipo ndinauza Alevi kuti adziyeretse, nabwere, nasunge pazipata kupatula dzuwa la Sabata. Mundikumbukire Icinso, Mulungu wanga, ndi kundileka monga mwa cifundo canu cacikuru.

23. Masiku aja ndinaonanso Ayudawo anadzitengera akazi a Asidodi, Aamoni, ndi Amoabu,

24. ndi ana ao analankhula mwina Ciasidodi, osadziwitsa kulankhula Ciyuda, koma monga umo amalankhula mtundu wao uli wonse.

25. Ndipo ndinatsutsana nao, ndi kuwatemberera, ndi kukantha ena a iwo, ndi kumwetula tsitsi lao, ndi kuwalumbiritsa pa Mulungu ndi kuti, Musapereka ana anu akazi kwa ana ao amuna, kapena kutengera ana anu amuna, kapena a inu nokha, ana ao akazi.

26. Nanga Solomo mfumu ya Israyeli sanacimwa nazo zinthu izi? cinkana mwa amitundu ambiri panalibe mfumu ngati iye, ndi Mulungu wace anamkonda, ndi Mulungu wace anamlonga mfumu ya Aisrayeli onse; koma ngakhale iye, akazi acilendo anamcimwitsa.

27. Ndipo kodi tidzamvera inu, kucita coipa ici cacikuru conse, kulakwira Mulungu wathu ndi kudzitengera akazi acilendo?

28. Koma wina wa ana a Yoyada, mwana wa Eliasibu mkuru wa ansembe, anali mkamwini wa Sanibalati Mhoroni; cifukwa cace ndinampitikitsa kumcotsa kwa ine.

29. Muwakumbukile Mulungu wanga, popeza anadetsa unsembe, ndi pangano la unsembe, ndi la Alevi.

30. Momwemo ndinawayeretsa kuwacotsera acilendo onse, ndi kuikira udikiro ansembe ndi Alevi, yense ku nchito yace;

31. ndi copereka ca nkhuni pa nthawi zoikika, ndi wa zipatso zoyamba. Mundikumbukile, Mulungu wanga, cindikomere.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 13