Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Maliro 1:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ha! mudziwo unadzala anthu, ukhalatu pa wokha!Ukunga mkazi wamasiye!Waukuruwo mwa amitundu, kalonga wamkazi m'madera a dzikoWasanduka wolamba!

2. Uliralira usiku; misozi yace iri pa masaya ace;Mwa onse amene anaukonda mulibe mmodzi wakuutonthoza:Mabwenzi ace onse aucitira ziwembu,Asanduka adani ace.

3. Yuda watengedwa ndende cifukwa ca msauko ndi ukapolo waukuru;Akhala mwa amitundu, sapeza popuma;Onse akumlondola anampeza pakati popsinjikiza.

4. M'njira za Ziyoni mulira posoweka akudzera msonkhano;Pa zipata zace zonse papasuka; ansembe ace onse ausa moyo;Anamwali ace asautsidwa; iye mwini namva zowawa.

5. Amaliwongo ace asanduka akuru ace, adani ace napindula;Pakuti Yehova wamsautsa pocuruka zolakwa zace;Ana ace ang'ono alowa m'ndende pamaso pa adani ace.

6. Ulemu wace wonse wamcokera mwana wamkazi wa Ziyoni;Akalonga ace asanduka nswala zosapeza busa,Anayenda opanda mphamvu pamaso pa wompitikitsa.

7. M'masiku a msauko wace ndi kusocera kwaceYerusalemu ukumbukira zokondweretsa zace zonse zacikhalire;Pogwidwa anthu ace ndi mdaniyo popanda wakuupulumutsa,Adaniwo anamuona naseka mwacipongwe mabwinja ace.

8. Yerusalemu wacimwa kwambiri; cifukwa cace wasanduka cinthu conyansa;Onse akuulemekeza aupeputsa, pakuti auona wamarisece;Inde, uusa moyo, nubwerera m'mbuyo.

9. Udio wace unali m'nsaru zace; sunakumbukira citsiriziro cace;Cifukwa cace watsika mozizwitsa; ulibe wakuutonthoza;Taonani Yehova, msauko wanga, pakuti mdaniyo wadzikuzayekha.

10. Amaliwongo atambasulira manja ao pa zokondweretsa zace zonse;Pakuti waona amitundu atalowa m'malo ace opatulika,Amene munalamulira kuti asalowe mumsonkhano mwanu.

11. Anthu ace onse ausa moyo nafunafuna mkate;Ndi zokondweretsa zao agula zakudya kuti atsitsimutse moyo wao;Taonani, Yehova, nimupenye; pakuti ndasanduka wonyansa.

12. Kodi muyesa cimeneci cabe, nonsenu opita panjira?Penyani nimuone, kodi ciripo cisoni cina ngati cangaci amandimvetsa ine,Cimene Yehova wandisautsa naco tsiku la mkwiyo wace waukali?

13. Anatumiza moto wocokera kumwamba kulowa m'mafupa anga, unawagonjetsa;Wachera mapazi anga ukonde, wandibwezera m'mbuyo;Wandipululutsa ndi kundilefula tsiku lonse.

Werengani mutu wathunthu Maliro 1