Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 24:8-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Nthawi zonse tsiku la Sabata aukonze pamaso pa Yehova, cifukwa ca ana a Israyeli, ndilo pangano losatha.

9. Ndipo ukhale wa Aroni ndi ana ace, audye pamalo popatulika; pakuti auyese wopatulikitsa wocokera ku nsembe zamoto za Yehova; ndilo lemba losatha.

10. Ndipo mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeli, atate wace ndiye M-aigupto, anaturuka mwa ana a Israyeli; ndi mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeliyo analimbana naye munthu M-israyeli kucigono;

11. ndipo mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeli anacitira DZINA mwano, natemberera; ndipo anadza naye kwa Mose. Dzina la mai wace ndiye Selomiti, mwana wa Dibri, wa pfuko la Dani.

12. Ndipo anamsunga m'kaidi, kuti awafotokozere m'mene anenere Yehova.

13. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

14. Turuka naye wotembererayo kunja kwa cigono; ndipo onse adamumva aike manja ao pamutu pace, ndi khamu lonse limponye miyala afe.

15. Ndipo unene ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Ali yense wotemberera Mulungu wace azisenza kucimwa kwace.

16. Ndi iye wakucitira mwano dzina la Yehova, amuphe ndithu; khamu lonse limponye miyala ndithu; mlendo ndi wobadwa m'dziko yemwe akacitira dzina la Yehova mwano, awaphe.

17. Munthu akakantha munthu mnzace ali yense kuti afe, amuphe ndithu.

18. Munthu akakantha nyama kuti ife, ambwezere yina; moyo kulipa moyo.

19. Munthu akacititsa mnansi wace cirema, monga umo anacitira momwemo amcitire iye;

20. kutyola kulipa kutyola, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino; monga umo anacitira munthu cirema, momwemo amcitire iye.

21. Iye wakukantha nyama kuti ife, ambwezere yina; iye wakupha munthu, amuphe.

22. Ciweruzo canu cifanefane ndi mlendo ndi wobadwa m'dziko; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

23. Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, ndipo anaturutsa wotembererayo kunja kwa cigono, namponya miyala. Ndipo ana a Israyeli anacita monga Yehova adauza Mose.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 24