Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 3:6-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anaimirira, nandengulitsa dziko lapansi;Anapenya, nanjenjemeretsa amitundu;Ndi mapiri acikhalire anamwazika,Zitunda za kale lomwe zinawerama;Mayendedwe ace ndiwo a kale lomwe.

7. Ndinaona mahema a Kusani ali mkusauka;Nsaru zocinga za dziko la Midyani zinanjenjemera.

8. Kodi Yehova anaipidwa nayo mitsinje?Mkwiyo wanu unali pamitsinje kodi,Kapena ukali wanu panyanja,Kuti munayenda pa akavalo anu,Pa magareta anu a cipulumutso?

9. Munapombosola uta wanu;Malumbiro analumbirira mafuko anali mau oona.Munang'amba dziko lapansi ndi mitsinje.

10. Mapiri anakuonani, namva zawawa;Cigumula ca madzi cinapita;Madzi akuya anamveketsa mau ace,Nakweza manja ace m'mwamba.

11. Dzuwa ndi mwezi zinaima njera mokhala mwao;Pa kuunika kwa mibvi yanu popita iyo.Pa kung'anipa kwa nthungo yanu yonyezimira.

12. Munaponda dziko ndi kulunda,Munapuntha amitundu ndi mkwiyo.

13. Munaturukira cipulumutso ca anthu anu,Cipulumutso ca odzozedwa anu;Munakantha mutu wa nyumba yawoipa,Ndi kufukula maziko kufikira m'khosi.

14. Munapyoza ndi maluti ace mutu wa ankhondo ace;Anadza ngati kabvumvulu kundimwaza;Kukondwerera kwao kunanga kufuna kutha ozunzika mabisika.

15. Munaponda panyanja ndi akavaloanu,Madzi amphamvu anaunjikana mulu.

16. Ndinamva, ndi m'mimba mwanga munabwadamuka,Milomo yanga inanthunthumira pamau,M'mafupa mwanga mudalowa cibvundi, ndipo ndinanjenjemera m'malo mwanga;Kuti ndipumule tsiku lamsauko,Pamene akwerera anthu kuti ayambane nao ndi makamu.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 3