Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 9:11-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo ndidzakhazikitsa pangano langa pamodzi ndi inu; zamoyo zonse sizidzamarizidwanso konse ndi madzi a cigumula; ndipo sikudzakhalanso konse cigumula cakuononga dziko lapansi.

12. Ndipo anati Mulungu, Ici ndici cizindikiro ca pangano limene ndipangana ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse ziti pamodzi ndi inu, ku mibadwo mibadwo;

13. ndiika Uta-wa-Leza wanga m'mtambomo, ndipo udzakhala cizindikiro ca pangano lopangana ndi Ine ndi dziko lapansi.

14. Ndipo padzakhala popimba ndi mtambo Ine dziko lapansi, utawo udzaoneka m'mtambomo;

15. ndipo ndidzakumbukira pangano langa limene liri ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo; ndipo madzi sadzakhalanso konse cigumula cakuononga zamoyo zonse.

16. Ndipo utawo udzakhala m'mtambo; ndipo ndidzauyang'anira kuti ndikumbukire pangano lacikhalire liri ndi Mulungu ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo pa dziko lapansi.

17. Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Ici ndici cizindikiro ca pangano ndalikhazikitsa popaogana ndi Ine ndi zamoyo zonse za pa dziko lapansi.

18. Ndi ana amuna a Nowa amene anaturuka m'cingalawa ndiwo Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti: Hamu ndiye atate wace wa Kanani.

19. Amenewa ndiwo ana amuna atatu a Nowa: ndiwo anafalikira dziko lonse lapansi.

20. Ndipo anayamba Nowa kukhala munthu wakulima nthaka, ndipo analima munda wamphesa:

21. namwa vinyo wace, naledzera; ndipo anali wamarisece m'kati mwa bema wace.

22. Ndipo Hamu atate wace wa Kanani, anauona umarisece wa atate wace, nauza abale ace awiri amene anali kunja.

23. Semu ndi Yafeti ndipo anatenga copfunda, naciika pa mapewa ao a onse awiri, nayenda cambuyo, napfunditsa umarisece wa atate wao: nkhope zao zinali cambuyo, osaona umarisece wa atate ao.

24. Nowa ndipo anauka kwa kuledzera kwace, nadziwa cimene anamcitira iye mwana wace wamng'ono.

Werengani mutu wathunthu Genesis 9