Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 8:7-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ndipo anaturutsa khungubwe, ndipo anaturuka kunka kwina ndi kwina kufikira adaphwa madzi pa dziko lapansi,

8. Ndipo anaturutsa njiwa imcokere, kuti aone kapena madzi anaphwa pamwamba pa dziko lapansi;

9. koma njiwayo siinapeza popondapo phazi lace, nibwera kwa iye kucingalawako, pakuti madzi analipo pa dziko lonse lapansi; ndipo anaturutsa dzanja lace, naitenga, nailowetsa kwa iye m'cingalawamo.

10. Ndipo analinda masiku ena asanu ndi awiri; naturutsanso njiwayo m'cingalawamo;

11. ndipo njiwa inadza kwa iye madzulo; ndipo, taonani, m'kamwa mwace munali tsamba lazitona lotyoledwa: ndipo anadziwa Nowa kuti madzi analimkuphwa pa dziko lapansi.

12. Ndipo analindanso masiku ena asanu ndi awiri; naturutsa njiwayo: ndipo siinabweranso konse kwa iye.

13. Ndipo panali caka ca mazana asanu ndi limodzi kudza cimodzi, mwezi woyamba, tsiku loyamba mwezi, madzi anaphwa pa dziko lapansi; ndipo Nowa anacotsa cindwi lace pacingalawa, nayang'ana, ndipo taonani, padauma pa dziko lapansi.

14. Mwezi waciwiri tsiku la makumi awiri kudza asanu ndi awiri la mwezi, lidauma dziko lapansi.

15. Mulungu ndipo ananena kwa Nowa, kuti,

16. Turukamoni m'cingalawamo, iwe ndi ana ako, ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.

17. Turutsa pamodzi ndi iwe zamoyo zonse ziti ndi iwe za nyama zonse, zouluka, ndi zinyama, ndi zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi; kuti ziswane pa dziko lapansi, zibalane, zicuruke pa dziko lapansi.

18. Ndipo anaturuka Nowa ndi ana ace, ndi mkazi wace, ndi akazi a ana ace, pamodzi naye:

19. zinyama zonse, zokwawa zonse, zouluka zonse, ndi zonse zokwawa pa dziko lapansi, monga mwa mitundu yao, zinaturuka m'cingalawamo.

20. Ndipo Nowa anamanga guwa la nsembe la Yehova; natengapo nyama zodyedwa zonse ndi mbalame zodyedwa zonse napereka nsembe zopsereza paguwapo.

21. Ndipo Yehova anamva conunkhira cakukondweretsa; nati Yehova m'mtima mwace, Sindidzatembereranso konse nthaka cifukwa ca munthu; pakuti ndingaliro ya mtima wa munthu iri yoipa kuyambira pa unyamata wace; sindidzaphanso konse zinthu zonse zamoyo, monga momwe ndacitiramo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 8