Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 27:36-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Ndipo iye anati, Kodi si ndico cifukwa anamucha dzina lace Yakobo? kuti wandinyenga ine kawiri aka; analanda ukulu wanga ndipo taonani, tsopano walanda mdalitso wanga. Ndipo anati, Kodi smunandisungira ine mdalitso?

37. Ndipo anayankha Isake nati kwa Esau, paona, ndamuyesa iye mkuru wako, ndi abale ace onse ndampatsa iye akhale akapolo ace; ndakhazikitsa iye ndi tirigu ndi vinyo; nanga pamenepo mwana wanga, ndidzakucitira iwe ciani?

38. Ndipo Esau anati kwa atate wace, Kodi muli nao mdalitso umodzi wokha, atate wanga? Mundidalitse ine, inenso, atate wanga, Ndipo Esau anakweza mau ace nalira.

39. Ndipo Isake atate wace anayankha nati kwa iye,Taona, pokhala pako mpa zonenepa za dziko lapansi,Mpa mame a kumwamba akudzera komwe;

40. Udzakhala ndi moyo ndi lupanga lako, nudzakhala kapolo wamphwako;Ndipo padzakhalapamene udzapulumuka,Udzacotsa gori lace pakhosi pako.

41. Ndipo Esau anamuda Yakobo cifukwa ca mdalitso umene atate wace anamdalitsa nao: ndipo Esau anati m'mtima mwace, Masiku a maliro a atate wanga ayandikira; pamenepo ndipo ndidzamupha mphwanga Yakobo.

42. Ndipo anauza Rebeka mau a Esau mwana wace wamkuru: ndipo iye anatumiza naitana Yakobo mwana wace wamng'ono, nati kwa iye, Taona, mkuru wako Esau, kunena za iwe, adzitonthoza yekha mtima wace kuti adzakupha iwe.

43. Ndipo tsopane mwana wanga, tamvera mau anga: tauka, nuthawire kwa Labani mlongo wanga ku Harana;

Werengani mutu wathunthu Genesis 27