Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 24:54-66 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

54. Ndipo anadya namwa iye ndi anthu amene anali pamodzi naye, nagonapo usiku: ndipo anauka m'mamawa, ndipo iye anati, Mundilole ine ndinke kwa mbuyanga.

55. Ndipo mlongo wace ndi amace anati, Namwali akhale ndi ife masiku akuwerengeka, afikire khumi; patsogolo pace iye adzamuka.

56. Ndipo iye anati kwa iwo, Musandicedwetse ine, pakuti Yehova wandiyendetsa bwino m'njira yanga: mundilole ine ndinke kwa mbuyanga.

57. Ndipo anati iwo, Tidzamuitana namwaliyo, tidzamfunsa pakamwa pace.

58. Ndipo anamuitana Rebeka nati kwa iye, Kodi udzanka pamodzi ndi munthuyo? Ndipo anati, Ndidzanka.

59. Ndipo anamlola Rebeka mlongo wao ndi mlezi wace, amuke pamodzi ndi mnyamata wace wa Abrahamu, ndi anthu ace.

60. Ndipo anamdalitsa Rebeka, nati kwa iye, Mlongo wathu ndiwe, iwe ukhale amai wa anthu zikwizikwi, mbeu zako zigonjetse cipata ca iwo akudana nao.

61. Ndipo adauka Rebeka ndi anamwali ace, nakwera pa ngamila natsata munthuyo: mnyamatayo ndipo anamtenga Rebeka namuka.

62. Ndipo Isake anadzera njira ya Beereahai-roi; cifukwa kuti anakhala iye n'dziko la kumwera.

63. Ndipo Isake anaturuka kulingalira m'munda madzulo; ndipo anatukula maso ace, nayang'ana, taona, ngamila zinalinkudza,

64. Ndipo Rebeka anatukula maso ace, ndipo pamene anaonalsake anatsika pa ngamila,

65. Ndipo anati kwa mnyamata, Munthuyo ndani amene ayenda m'munda kukomana ndi ife? Mnyamatayo ndipo anati, Uyo ndi mbuyanga: cifukwa cace namwali anatenga cophimba cace nadziphimba.

66. Mnyamatayo ndipo anamuuza Isake zonse anazicita.

Werengani mutu wathunthu Genesis 24