Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 44:17-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo kudzatero, polowa iwo ku zipata za bwalo lam'kati abvale zobvala zabafuta; koma zaubweya asazibvale ponditumikira Ine m'zipata za bwalo la m'kati, ndi m'kacisi.

18. Akhale nao akapa abafuta pamitu pao, ndi akabudula m'cuuno mwao; asabvale m'cuuno kanthu kali konse kakucititsa thukuta.

19. Ndipo akaturukira ku bwalo lakunja, ku bwalo lakunja kuti anthu, azibvula zobvala zao zimene atumikira nazo, naziike m'zipinda zopatulika, nabvale zobvala zina; angapatule anthu ndi zovala zao.

20. Ndipo asamete mitu yao, kapena asalekerere nzera za tsitsi lao zikule, azingosenga mitu yao.

21. Kungakhale kumwa vinyo, wansembe asamwe polowa ku bwalo la m'katimo.

22. Kungakhale kutenga amasiye kapena osudzulidwa akhale akazi ao, asacite; koma atenge anamwali a mbeu ya nyumba ya Israyeli, kapena wamasiye ndiye wamasiye wa wansembe.

23. Ndipo aziphunzitsa anthu anga asiyanitse pakati pa zopatulika ndi zinthu wamba, ndi kuwazindikiritsa pakati pa zodetsa ndi zoyera.

24. Ndipo pakakhala mlandu, aimeko kuweruza; auweruze monga mwa maweruzo anga, ndipo azisunga malamulo anga, ndi malemba anga, pa madyerero anga onse oikika; napatulikitse masabata anga.

25. Ndipo asayandikire kwa munthu ali yense wakufa, angadzidetse; koma cifukwa ca atate, kapena mai, kapena mwana wamwamuna, kapena mwana wamkazi, kapena mbale, kapena mlongo wopanda mwamuna, nkuloleka kudzidetsa.

26. Ndipo atayeretsedwa amwerengere masiku asanu ndi awiri.

27. Ndipo tsiku loti alowa m'malo opatulika, bwalo lam'kati, kutumikira m'malo opatulika, apereke nsembe yace yaucimo, ati Ambuye Yehova.

28. Ndipo adzakhala naco colowa; Ine ndine colowa cao; musawapatsa colandira cao m'Israyeli; Ine ndine colandira cao.

29. Azidya nsembe yaufa, ndi nsembe yaucimo, ndi nsembe yoparamula; ndipo ziri zonse zoperekedwa ciperekere m'Israyeli ndi zao.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 44