Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 10:12-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo unayankha msonkhano wonse, ndi kunena ndi mau akuru, Monga mwa mau anu tiyenera kucita.

13. Koma anthu ndiwo ambiri, ndi nyengo yino nja mvula, tiribenso mphamvu yakuima pabwalo, ndi nchitoyi sindiyo ya tsiku limodzi kapena awiri; pakuti tacurukitsa kulakwa kwathu pa cinthu ici.

14. Ayang'anire ici tsono akalonga athu a msonkhano wonse, ndi onse a m'midzi mwathu amene anadzitengera akazi acilendo abwere pa nthawi zoikika, ndi pamodzi nao akuru a mudzi wao uli wonse, ndi oweruza ace, mpaka udzaticokera mkwiyo waukali wa Mulungu wathu cifukwa ca mlandu uwu.

15. Yonatani mwana wa Asaheli ndi Yazeya mwana wa Tikiva okha anatsutsana naco, ndi Mesulamu ndi Sabetai Mlevi anawathandiza.

Werengani mutu wathunthu Ezara 10