Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 36:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo aluso onse, akucita nchito yonse ya malo opatulika, anadza onse ndi kusiya nchito yao: analinkucita;

5. nanena ndi Mose, ndi kuti, Anthu alinkubwera nazo zocuruka, zakuposera zoyenera nchito imene Yehova anauza icitike.

6. Ndipo Mose analamulira, ndipo anamveketsa mau mwa cigono conse, ndi kuti, Asaonjezere nchito ya ku copereka ca malo opatulika, ngakhale mwamuna ngakhale mkazi. Tero anawaletsa anthu asabwere nazo zina.

7. Popeza zipangizo zinakwanira nchito yonse icitike, zinatsalakonso.

8. Ndipo onse a mtima waluso mwa iwo akucita nchitoyi anapanga kacisi ndi nsaru zophimba khumi; anaziomba ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi lamadzi; ndi lofiira, ndi lofiira, ndi akerubi, nchito ya mmisiri.

9. Utali wace wa nsaru yophimba imodzi ndiwo mikono makumi awiri kudza isanu ndi itatu, ndi kupingasa kwace kwa nsaru imodzi mikono inai; nsaru zonse zinafanana muyeso wao.

10. Ndipo analumikiza nsaru zisanu yina ndi inzace; nalumikiza nsaru zisanu zina yina ndi inzace.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 36