Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 18:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Tsopano ndidziwa kuti Yehova ali wamkuru ndi milungu yonse; pakuti momwe anadzikuza okha momwemo anawaposa,

12. Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anamtengera Mulungu nsembe Yopsereza, ndi nsembe zophera; ndipo Aroni ndi akuru onse a Israyeli anadza kudzadya mkate ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.

13. Ndipo kunatero kuti m'mawa mwace Mose anakhala pansi kuweruzira anthu mirandu yao; ndipo anthu anakhala ciriri pamaso pa Mose kuyambira m'mawa kufikira madzulo.

14. Ndipo pamene mpongozi wace wa Mose anaona zonsezi iye anawacitira anthu, anati, Cinthu ici nciani uwacitira anthuci? Umakhala pa wekha bwanji, ndi anthu onse amakhala ciriri pamaso pako kuyambira m'mawa kufikira madzulo?

15. Ndipo Moce anati kwa mpongozi wace, Cifukwa anthu amadza kwa ine kudzafunsira Mulungu;

16. akakhala nao mlandu adza kwa ine, kuti ndiweruze pakati pa munthu ndi mnansi wace, ndi kuti ndiwadziwitsemalemba a Mulungu, ndi malamulo ace.

17. Koma mpongozi wa Mose ananena naye, Cinthu ucitaci siciri cabwino ai.

18. Udzalema konse, iwe ndi anthu amene uli nao; pakuti cikulaka cinthu ici; sungathe kucicita pa wekha.

19. Tamvera mau anga tsopano, ndikupangire nzeru, ndi Mulungu akhale nawe; ukhale m'malo mwa anthu kwa Mulungu, nupite nayo mirandu kwa Mulungu;

20. nuwamasulire malemba, ndi malamulo, ndi kuwadziwitsa njira imene ayenera kuyendamo, ndi nchito imene ayenera kucita.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 18