Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 15:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pakuti akavalo a Farao analowa m'nyanja, ndi magareta ace ndi apakavalo ace, ndipo Yehova anawabwezera madzi a m'nyanja; koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja.

20. Ndipo Miriamu mneneriyo, mlongo wa Aroni, anagwira lingaka m'dzanja lace; ndipo akazi onse anaturuka kumtsata ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe.

21. Ndipo Miriamu anawayankha,Yimbirani Yehova, pakuti wapambanatu;Kavalo ndi wokwera wace anawaponya m'nyanja.Madzi a ku Mara.

22. Ndipo Mose anatsogolera Israyeli kucokera ku Nyanja Yofiira, ndipo anaturukako nalowa m'cipululu ca Suri; nayenda m'cipululu masiku atatu, osapeza madzi.

23. Pamene anafika ku Mara, sanakhoza kumwa madzi a Mara, pakuti anali owawa; cifukwa cace anacha dzina lace Mara.

24. Ndipo anthu anadandaulira Mose, ndi kuti, Tidzamwa ciani?

25. Ndipo iye anapfuulira kwa Yehova; ndipo Yehova anamsonyeza mtengo ndipo anauponya m'madzimo, ndi madzi anasanduka okoma. Pamenepo anawapangira lemba ndi ciweruzo, ndi pomwepa anawayesa;

26. ndipo anati, Ngati udzamveratu mau a Yehova, Mulungu wako, ndi kucita zoona pamaso pace, ndi kuchera khutu pa malamulo ace, ndi kusunga malemba ace onse, za nthenda zonse ndinaziika pa Aaigupto sindidzaziika pa iwe nnena imodzi; pakuti Ine Yehova ndine wakuciritsa iwe.

27. Ndipo anafika pa Elimu, ndi pamenepo panali akasupe a madzi khumi ndi awiri, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; ndipo anamanga cigono cao pomwepo pa madziwo.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 15