Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 14:3-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Farao adzanena za ana a Israyeli, Azimidwa dziko, cipululu cawatsekera.

4. Ndipo ndidzalimbitsa mtima wace wa Farao kuti awalondole; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao ndi pa nkhondo yace yonse; pamenepo Aaigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, Ndipo anacita comweco.

5. Ndipo anauza mfumu ya Aigupto kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ace inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ici nciani tacita, kuti talola Israyeli amuke osatigwiriranso nchito?

6. Ndipo anamanga gareta lace, napita nao anthu ace;

7. napita nao magareta osankhika mazana asanu ndi limodzi, ndi magareta onse a m'Aigupto, ndi akapitao ao onse.

8. Ndipo Yehova analimbitsa mtima wa Farao, mfumu ya Aigupto, ndipo iye analondola ana a Israyeli; koma ana a Israyeli adaturuka ndi dzanja lokwezeka.

9. Ndipo Aaigupto anawalondola, ndiwo akavalo ndi magareta onse a Farao, ndi apakavalo ace, ndi nkhondo yace, nawapeza ali kucigono kunyanja, pa Pihahiroti, patsogolo pa Baala-Zefoni.

10. Ndipo pamene Farao anayandikira ana a Israyeli anatukula maso ao, taonani, Aaigupto alinkutsata pambuyo pao; ndipo anaopa kwambiri; ndi ana a Israyeli anapfuulira kwa Yehova.

11. Ndipo anati kwa Mose, Kodi mwaticotsera kuti tikafe m'cipululu cifukwa panahbe manda m'Aigupto? Nciani ici mwaticitira kuti mwatiturutsa m'Aigupto?

12. Si awa maowo tinalankhula nanu m'Aigupto ndi kuti, Tliekeni, kuti tigwirire nchito Aaigupto? pakuti kutumikira Aaigupto kutikomera si kufa m'cipululu ai.

13. Ndipo Mose ananena ndi anthu, Musaope, cirimikani, ndipo penyani cipulumutso ca Yehova, cimene adzakucitirani lero; pakuti Aaigupto mwawaona lerowa simudzawaonansokonse.

14. Yehova adzakugwirirani nkhondo, ndipo inu mudzakhala cere.

15. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Upfuuliranji kwa Ine? lankhula ndi ana a Israyeli kuti aziyenda.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 14