Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 24:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Munthu akatenga mkazi akhale wace, kudzali, ngati sapeza ufulu pamaso pace, popeza anapeza mwa iye kanthu kosayenera, amlembere kalata wa cilekanitso, ndi kumpereka uyu m'dzanja lace, ndi kumturutsa m'nyumba mwace.

2. Ndipo ataturuka m'nyumba mwace, amuke nakhale mkazi wa mwamuna wina.

3. Ndipo akamuda mwamuna waciwiriyo, nakamlemberanso kalata wa cilekanitso, ndi kumpereka uyu m'dzanja lace, nakamturutsa m'nyumba mwace; kapena akamwalira mwamuna wotsirizayo, amene anamtenga akhale mkazi wace;

4. pamenepo mwamuna woyamba anamcotsayo sangathe kumtenganso akhale mkazi wace, atadetsedwa iye; pakuti ici ndi conyansa pamaso pa Yehova; ndipo usamacimwitsa dziko, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colandira canu.

5. Munthu akatenga mkazi watsopano, asaturuke nayo nkhondo, kapena asamcititse kanthu kali konse; akhale waufulu ku nyumba yace caka cimodzi, nakondweretse mkazi adamtengayo.

6. Munthu asalandire cikole mphero, ngakhale mwanamphero, popeza alandirapo cikole moyo wamunthu.

7. Akampeza munthu waba mbale wace wina wa ana a Israyeli, namuyesa kapolo, kapena wamgulitsa, afe wakubayo; potero muzicotsa coipaco pakati panu.

8. Cenjerani nayo nthenda yakhate, kusamaliratu, ndi kucita monga mwa zonse akuphunzitsani ansembe Alevi; monga ndinalamulira iwo, momwemo muzisamalira kucita.

9. Kumbukilani cimene Yehova Mulungu wanu anacitira Miriamu panjira, poturuka inu m'dziko la Aigupto.

10. Mukakongoletsa mnansi wanu ngongole iri yonse, musamalowa m'nyumba mwace kudzitengera cikole cace.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 24