Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 16:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo muiphike ndi kuidya m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha; koma m'mawa mwace mubwerere kumka ku mahema anu.

8. Masiku asanu ndi limodzi muzidya mkate wopanda cotupitsa; ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo loletsa, la Yehova Mulungu wanu; musamagwira nchito pamenepo.

9. Mudziwerengere masabata asanu ndi awiri; muyambe kuwerenga masabata asanu ndi awiri poyambira kuceka tirigu waciriri.

10. Ndipo mucitire Yehova Mulungu wanu madyerero a masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.

11. Ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi wokhala m'mudzi mwanu, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala pakati pa inu, m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lace.

12. Ndipo mukumbukire kuti munali akapolo m'Aigupto; musamalire kucita malemba awa.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 16