Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 16:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. nimukondwere m'madyerero mwanu, inu, ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye okhala m'mudzi mwanu.

15. Masiku asanu ndi awiri mucitire Yehova Mulungu wanu madyerero m'malo amene Yehova adzasankha; popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m'zipatso zanu zonse, ndi m'nchito zonse za manja anu; nimukondwere monsemo.

16. Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'malo amene iye adzasankha, katatu m'caka; pa madyerero a mkate wopanda cotupitsa, pa madyerero a masabata, ndi pa madyerero a misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;

17. apereke yense monga mwa mphatso ya m'dzanja lace, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani.

18. Mudziikire oweruza ndi akapitao m'inidzi yanu yonse imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, monga mwa mapfuko anu; ndipo aweruze anthu ndi ciweruzo colungama.

19. Musamapotoza ciweruzo, musamasamalira munthu, kapena kulandira cokometsera mlandu; popeza cokometsera mlandu cidetsa maso a anzeru, niciipsa mau a olungama.

20. Cilungamo, cilungamo ndico muzicitsata, kuti mukhale ndi moyo ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 16