Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 2:18-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. kuti apemphe zacifundo kwa Mulungu wa Kumwamba pa cinsinsi ici; kuti Danieli ndi anzace asaonongeke pamodzi ndi eni nzeru ena a ku Babulo.

19. Pamenepo cinsinsico cinabvumbulutsidwa kwa Danieli m'masomphenya a usiku. Ndipo Danieli analemekeza Mulungu wa Kumwamba.

20. Danieli anayankha, nati, Lilemekezedwe dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi, a pakuti nzeru ndi mphamvu ziri zace;

21. pakuti amasanduliza nthawi ndi nyengo, acotsa mafumu, nalonga mafumu, apatsa anzeru nzeru, ndi cidziwitso kwa iwo okhoza kuzindikira.

22. Iye abvumbulutsa zinthu zakuya ndi zinsinsi; adziwa zokhala mumdima, ndi kuunika kumakhala kwa Iye.

23. Ndikuyamikani ndi kukulemekezani Inu, Mulungu wa makolo anga, pakuti mwandipatsa nzeru ndi mphamvu; ndipo mwandidziwitsa tsopano ici tacifuna kwa Inu; pakuti mwatidziwitsa mlandu wa mfumu.

24. Potero Danieli analowa kwa Arioki amene mfumu idamuika aononge eni nzeru a ku Babulo; anamuka, natero naye, Usaononga eni nzeru a ku Babulo, undilowetse kwa mfumu, ndipo ndidzaululira mfumu kumasulirako.

25. Pamenepo Arioki analowa naye Danieli kwa mfumu mofulumira; natero nayo, Ndapeza munthu wa ana a ndende a Yuda, ndiye adzadziwitsa mfumu kumasulira kuja.

26. Mfumu inayankha, niti kwa Danieli, amene dzina lace ndiye Belitsazara, Ukhoza kodi kundidziwitsa lotolo ndidalilota, ndi kumasulira kwace?

27. Nayankha Danieli pamaso pa mfumu, nati, Cinsinsi inacitira liuma mfumu, angakhale anzeru, openduza, alembi, kapena alauli, sakhoza kuciululira mfumu;

28. koma kuli Mulungu Kumwamba wakubvumbulutsa zinsinsi; Iye ndiye wadziwitsa mfumu Nebukadinezara cimene cidzacitika masiku otsiriza. Loto lanu, ndi masomphenya a m'mtima mwanu pakama panu, ndi awa:

29. Inu mfumu, maganizo anu analowa m'mtima mwanu muli pakama panu, akunena za ico cidzacitika m'tsogolomo; ndipo Iye amene abvumbulutsa zinsinsi wakudziwitsani codzacitikaco.

30. Koma ine, cinsinsi ici sicinabvumbulutsidwa kwa ine cifukwa ca nzeru ndiri nayo yakuposa wina ali yense wamoyo, koma kuti kumasuliraku kudziwike kwa mfumu, ndi kuti mudziwe maganizo a mtima wanu.

31. Inu mfumu munapenya ndi kuona fano lalikuru. Fanoli linali lalikuru, ndi kunyezimira kwace kunaposa; linali kuima popenyana ndi inu, ndi maonekedwe ace anali oopsa,

Werengani mutu wathunthu Danieli 2