Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 5:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Comweco akuru onse a Israyeli anadza kwa mfumu ku Hebroni; ndipo mfumu Davide anapangana nao pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova; ndipo anamdzoza Davide mfumu ya Israyeli.

4. Davide anali ndi zaka makumi atatu polowa iye ufumu wace, nakhala mfumu zaka makumi anai.

5. Ku Hebroni anacita ufumu pa Yuda zaka zisanu ndi ziwiri kudza miyezi isanu ndi umodzi; ndi ku Yerusalemu anacita ufumu pa Aisrayelionse ndi Ayuda omwe zaka makumi atatu mphambu zitatu.

6. Ndipo mfumu ndi anthu ace anamuka ku Yerusalemu kuyambana nao Ajebusi, nzika za dziko; ndiwo ananena kwa Davide ndi kuti, Sudzalowa muno, koma akhungu ndi opunduka adzakupitikitsa; ndiko kunena kuti, Davide sakhoza kulowa muno.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 5