Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 20:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pamene anafika iwo pa mwala waukuru uli ku Gibeoni, Amasa anadza kukomana nao. Ndipo Yoabu atabvala mwinjiro wace, anadzimangirira lamba lolongamo lupanga m'cimace m'cuuno mwace; ndipo m'kuyenda kwace lidasololoka.

9. Ndipo Yoabu ananena ndi Amasa, Uli bwino mbale wanga? Ndipo Yoabu anagwira ndebvu za Amasa ndi dzanja lace lamanja kuti ampsompsone.

10. Koma Amasa sanasamalira lupanga liri m'dzanja la Yoabu; comweco iye anamgwaza nalo m'mimba; nakhuthula matumbo ace pansi, osamgwazanso; nafa iye, Ndipo Yoabu ndi Abisai mbale wace analondola Seba mwana wa Bikri.

11. Ndipo mnyamata wina wa Yoabu anaima pali iye, nati, Wobvomereza Yoabu, ndi iye amene ali wace wa Davide, atsate Yoabu.

12. Ndipo Amasa analikukunkhulira m'mwazi wace pakati pa mseu. Ndipo pamene munthuyo anaona kuti anthu onse anaima, iye ananyamula Amasa namcotsa pamseu kumka naye kuthengo, nampfunda ndi cobvala, pamene anaona kuti anaima munthu yense wakufika pali iye.

13. Atamcotsa iye mumseu, anthu onse anapitirira kumsata Yoabu kukalondola Seba mwana wa Bikri.

14. Ndipo anapyola mapfuko onse a Israyeli kufikira ku Abeli ndi ku Betimaaka, ndi kwa Aberi onse; iwo nasonkhana pamodzi namlondolanso.

15. Ndipo anadza nammangira misasa m'Abeli wa Betimaaka, naundira nthumbira pa mudziwo, ndipo unagunda tioga; ndipo anthu onse akukhala ndi Yoabu anakumba lingalo kuti aligwetse.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 20