Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 30:5-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Motero anakhazikitsa mau kulalikira mwa Israyeli lonse, kuyambira Beereseba kufikira ku Dani, kuti abwere kucitira Yehova Mulungu wa Israyeli Paskha ku Yerusalemu; pakuti nthawi yaikuru sanacita monga mudalembedwa.

6. Tsono amtokoma anamuka ndi akalata ofuma kwa mfumu ndi akuru ace mwa Israyeli ndi Yuda lonse, monga inauza mfumu ndi kuti, Inu ana a Israyeli, bwerani kwa Yehova Mulungu wa Abrahamu, Isake, ndi Israyeli, kuti Iye abwere kwa otsala anu opulumuka m'dzanja la mafumu a Asuri.

7. Ndipo musamakhala ngati makolo anu ndi abale anu, amene anai akwira Yehova Mulungu wa makolo ao, motero kuti anawapereka apasuke, monga mupenya,

8. Musamakhala ouma khosi monga makolo anu; koma gwiranani dzanja ndi Yehova, nimulowe m'malo ace opatulika, amene anapatula kosatha, ndi kutumikira Yehova Mulungu wanu; kuti mkwiyo wace waukali utembenuke kwa inu.

9. Pakuti mukabwera kwa Yehova, abale anu ndi ana anu adzapeza cifundo pamaso pa iwo anawatenga ndende, nadzalowanso m'dziko muno; pakuti Yehova Mulungu wanu ngwa cisomo ndi cifundo; sadzakuyang'anirani kumbali ngati mubwera kwa Iye,

10. Ndipo amtokoma anapitira m'midzi m'midzi mwa dziko la Efraimu ndi Manase, mpaka Zebuloni; koma anawaseka pwepwete nawanyodola.

11. Komatu ena a Aseri ndi Manase ndi a Zebuloni anadzicepetsa, nadza ku Yerusalemu.

12. Ku Yuda komwe kunali dzanja la Mulungu lakuwapatsa mtima umodzi, kucita cowauza mfumu ndi akuru mwa mau a Yehova.

13. Nasonkhana ku Yerusalemu anthu ambiri kucita madyerero a mkate wopanda cotupitsa mwezi waciwiri, msonkhano waukuru ndithu.

14. Ndipo anauka nacotsa maguwa a nsembe okhala m'Yerusalemu, nacotsa pofukizira zonunkhira, naziponya m'mtsinje wa Kedroni.

15. Pamenepo anaphera Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi waciwiri, ndipo ansembe ndi Alevi anacita manyazi, nadzipatula, nabwera nazo nsembe zopsereza ku nyumba ya Yehova.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 30