Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 29:11-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ana anga, musazengereza tsopano; popeza Yehova anakusankhani inu muime pamaso pace, kumtumikira Iye, ndi kuti mukhale atumiki ace ndi kufukiza zonunkhira.

12. Pamenepo ananyamuka Alevi, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoeli mwana wa Azariya, a ana a Akohati; ndi a ana a Merari, Kisi mwana wa Abidi, ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; ndi a Agerisoni, Yowa mwana wa Zima, ndi Edeni mwana wa Yowa;

13. ndi a ana a Elizafana, Simri ndi Yeueli; ndi a ana a Asafu, Zekariya ndi Mataniya;

14. ndi a ana a Hemani, Yehudi ndi Simei ndi a ana a Yedutuni, Semaya ndi Uziyeli,

15. Ndipo anamemeza abale ao, nadzipatula, nalowa monga adawauza mfumu mwa mau a Yehova, kuyeretsa nyumba ya Yehova.

16. Ndipo ansembe analowa m'kati mwace mwa nyumba ya Yehova kuiyeretsa, naturutsira ku bwalo la nyumba ya Yehova zoipsa zonse anazipeza m'Kacisi wa Yehova. Nazilandira Alevi, kuziturutsira kunja ku mtsinje wa Kedroni.

17. Anayamba tsono kuipatula tsiku loyamba la mwezi woyamba, nafikira ku likole la Yehova tsiku lacisanu ndi citatu la mwezi, naipatula nyumba ya Yehova m'masiku asanu ndi atatu; natsiriza tsiku lakhumi ndi cisanu ndi cimodzi.

18. Pamenepo analowa m'katimo kwa mfumu Hezekiya, nati, Tayeretsa nyumba yonse ya Yehova, ndi guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zace zonse, ndi gome la mkate woonekera, ndi zipangizo zace zonse.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 29