Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 23:29-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Masiku ace Farao-Neko mfumu ya Aigupto anakwerera mfumu ya Asuri ku mtsinje wa Firate; Ddipo mfumu Yosiya anaturuka kuponyana naye, koma anapha Yosiya ku Megido, atamuona.

30. Ndipo anyamata ace anamtengera wakufa m'gareta, nabwera naye ku Yerusalemu kucokera ku Megido, namuika m'manda ace ace. Ndipo anthu a m'dziko anatenga Yoahazi mwana wa Yosiya, namdzoza, namlonga ufumu m'malo mwa atate wace.Yoahazi, Yoyakimu ndi Yoyakini mafumu oipa a Yuda.

31. Yoahazi anali wa zaka makumi awiri mphambu zitatu polowa ufumu wace, nakhala mfumu miyezi itatu m'Yerusalemu ndi dzina la mace ndiye Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.

32. Nacita iye coipa pamaso pa Yehova, monga umo monse adacita makolo ace.

33. Ndipo Faraoneko anammanga m'Ribila, m'dziko la Hamati; kuti asacite ufumu m'Yerusalemu; nasonkhetsa dzikoli msonkho wa matalente zana limodzi la siliva, ndi talente limodzi la golidi.

34. Ndipo Farao-Neko analonga ufumu Eliyakimu mwana wa Yosiya, m'malo mwa Yosiya atate wace, nasanduliza dzina lace likhale Yoyakimu; koma anapita naye Yoahazi, nafika iye m'Aigupto, nafa komweko.

35. Ndipo Yoyakimu anapereka siliva ndi golidi kwa Farao, koma anasonkhetsa dzikoli lipereke ndalamazi; monga mwa lamulo la Farao anasonkhetsa anthu a m'dziko siliva ndi golidi, yense monga mwa kuyesedwa kwace, kuzipereka kwa Farao-Neko.

36. Yoyakimu anali wa zaka makumi awiri ndi zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi ndi cimodzi m'Yerusalemu; ndi dzina la mace ndiye Zebida mwana wa Pedaya wa Ruma.

37. Nacita iye coipa pamaso pa Yehova, monga mwa zonse adazicita makolo ace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 23