Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 16:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Nthawi yomweyo Rezini mfumu ya Aramu anabwezera Elati kwa Aramu, napitikitsa Ayuda ku Elati; nadza Aaramu ku Elati, nakhala komweko kufikira lero lino.

7. Ndipo Ahazi anatuma mithenga kwa Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri, ndi kuti, Ine ndine kapolo wanu ndi mwana wanu; kwerani, mudzandipulumutse m'dzanja la mfumu ya Aramu, ndi m'dzanja la mfumu ya Israyeli anandiukirawo.

8. Natenga Ahazi siliva ndi golidi wopezeka m'nyumba ya Yehova, ndi ku cuma ca nyumba ya mfumu, nazitumiza mtulo kwa mfumu ya Asuri.

9. Nimmvera mfumu ya Asuri, nikwera kumka ku Damasiko mfumu ya Asuri, niulanda, nipita nao anthu ace andende ku Kiri, nimupha Rezini.

10. Ndipo mfumu Ahazi anamuka ku Damasiko kukakomana ndi Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri, naona guwa la nsembe linali ku Damasiko; natumiza mfumu Ahazi kwa Uriya wansembe cithunzithunzi cace, ndi cifanizo cace, monga mwa mamangidwe ace onse.

11. Ndipo Uriya wansembe anamanga guwa la nsembelo, monga mwa zonse anazitumiza mfumu Ahazi zocokera ku Damasiko; momwemo Uriya wansembe analimanga asanabwere mfumu ku Damasiko.

12. Atafika mfumu kucokera ku Damasiko, anapenya mfumu guwa la nsembelo, nayandikiza mfumu ku guwa la nsembelo, napereka nsembe pomwepo.

13. Nafukiza nsembe yace yopsereza ndi nsemba yace yaufa, natsanulira nsembe yace yothira, nawaza mwazi wa nsembe zace zamtendere pa guwa la nsembelo,

14. Nalicotsa guwa la nsembe lamkuwa linali pamasopa Yehova, nalicotsa kukhomo la nyumba pakati pa guwa la nsembe lace ndi nyumba ya Yehova, naliikakumpotokwa guwa la nsembe lace.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 16