Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 30:10-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Davide anawalondola, iye ndi anthu mazana anai; koma anthu mazana awiri anatsala m'mbuyo, cifukwa analema, osakhoza kuoloka kamtsinje Besori.

11. Ndipo ena anapeza M-aigupto kuthengo, nabwera naye kwa Davide, nampatsa cakudya, nadya iye; nampatsanso madzi kumwa;

12. nampatsanso cigamphu ca ncinci ya nkhuyu ndi ncinci ziwiri za mphesa; ndipo atadya, moyo wace unabweranso mwa iye; pakuti adagona masiku atatu ndi usiku wao, osadya cakudya, osamwa madzi.

13. Pamenepo Davide ananena naye, Ndiwe wa yani? ufumira kuti? Nati iye, Ndiri mnyamata wa ku Aigupto, kapolo wa M-amaleki; mbuye wanga anandisiya, cifukwa ndinayambodwala apita masiku atatu.

14. Tinathira nkhondo kumwera kwa Akereti ndi ku dziko lija la Ayuda, ndi kumwera kwa Kalebi; ndipo tinatentha mudzi wa Zikilaga ndi moto.

15. Ndipo Davide ananena naye, Kodi udzanditsogolera kufikira ku khamulo? Nati iye, Mundilumbirire kwa Mulungu, kuti simudzandipha, kapena kundipereka m'dzanja la mbuye wanga, ndipo ndidzatsika nanu kuli khamu limene.

16. Ndipo pamene anatsika naye, onani, iwo anabalalika apo ponse, analinkudya, ndi kumwa, ndi kudyerera, cifukwa ca cofunkha zambiri anazitenga ku dziko la Afilisti, ndi ku dziko la Yuda.

17. Ndipo Davide anawakantha kuyambira madzulo kufikira usiku wa mawa wace; ndipo panalibe munthu mmodzi wa iwowa anapulumuka, koma anyamata mazana anai oberekeka pa ngamila, nathawa.

18. Ndipo Davide analanditsa zonse anazitenga Aamaleki, napulumutsa akazi ace awiri.

19. Ndipo sikanasoweka kanthu, kakang'ono kapena kakakuru, ana amuna kapena ana akazi, kapena cuma kapena dna ciri conse ca zija anazitenga iwowa; Davide anabwera nazo zonse.

20. Ndipo Davide anatenga nkhosa zonse ndi ng'ombe zonse, zimene anazipitikitsa patsogolo pa zoweta zao zao, nati, Izi ndi zofunkha za Davide.

21. Ndipo Davide anafika kuli anthu mazana awiri amene analema osakhoza kutsata Davide, amenenso anawakhalitsa kukamtsinje Besori; ndipo iwowa anaturuka kucingamira Davide, ndi amene anali naye; ndipo pakuyandikira Davide anawafunsa ngati ali bwanji.

22. Pamenepo anthu oipa onse, ndi opanda pace a iwo amene anapita ndi Davide anayankha nati, Popeza sadamuka nafe sitidzawapatsa kanthu ka zofunkha tidazilanditsa, koma kwa munthu yense mkazi wace ndi ana ace, kuti acoke nao namuke.

23. Davide nati, Simudzatero, abale anga inu, ndi zimene anatipatsa ife Yehova, amene anatisunga, napereka m'dzanja lathu khamu lija linadza kumenyana nafe.

24. Ndipo ndani adzabvomerezana nanu mrandu uwu? Pakuti monga gawo lace la iye wakumuka kunkhondoko, momwemo lidzakhala gawo lace la iye wakukhala ndi akatundu, adzagawana cimodzimodzi.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 30