Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 20:1-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Davide anathawa ku Nayoti m'Rama, nadzanena pamaso pa Jonatani, Ndacitanji ine? kuipa kwanga kuli kotani? ndi chimo langa la pamaso pa atate wanu ndi ciani, kuti amafuna moyo wanga?

2. Namyankha, Usatero iai, sudzafa; ona, atate, wanga sacita kanthu kakakuru kapena kakang'ono wosandidziwitsa ine; atate wanga adzandibisiranji cinthu cimeneci? Si kutero ai.

3. Ndipo Davide analumbiranso nati, Atate wako adziwatu kuti wandikomera mtima; nati, Jonatani asadziwe ici, kuti angamve cisoni; koma pali Yehova, ndiponso pali moyo wako, pakati pa ine ndi imfa pali ngati phazilimodzi.

4. Ndipo Jonatani anati kwa Davide, Ciri conse mtima wako unena, ndidzakucitira.

5. Nati Davide kwa Jonatani, Onani, mawa mwezi ukhala, ndipo ine ndiyenera kupita kukadya kwa mfumu, wosatsala; koma undilole ndikabisale kuthengo, kufikira tsiku lacitatu madzulo ace.

6. Atate wako akandifuna pang'ono ponse, unene kuti, Davide anandiumirira ndimlole athamangire kwao ku Betelehemu, pakuti kumeneko kuli nsembe ya pacaka ya banja lao lonse.

7. Tsono akati, Cabwino; kapolo wako adzakhala ndi mtendere; koma akapsa mtima, uzindikirepo kuti anatsimikiza mtima kundicitira coipa.

8. Cifukwa cace ucitire kapolo wako zokoma mtima; popeza wamcititsa kapolo wako kupangana nawe pangano la kwa Yehova; koma ngati mwa ine muli coipa ciri conse, undiphe wekha; udzapita nane bwanji kwa atate wako?

9. Ndipo Jonatani anati, lai ndi pang'ono ponse; ine ndikadziwa konse kuti atate wanga anatsimikiza mtima kukucitira coipa, sindidzadziwitsa iwe kodi?

10. Tsono Davide anati kwa Jonatani, Adzandiuza ndani ngati atate wako alankhulira iwe mokalipa?

11. Nati Jonatani kwa Davide, Tiyeni timuke kuthengo. Namuka onse awiri kuthengoko.

12. Ndipo Jonatani anati kwa Davide, Yehova, Mulungu wa Israyeli, akhale mboni; nditaphera mwambi atate wanga mawa dzuwa lino, kapena mkuca, onani, pakakhala kanthu kabwino kakucitira Davide, sindidzakutumira mthenga ndi kukuululira kodi?

13. Mulungu alange Jonatani, ndi kuonjezapo, ngati atate wanga akondwera kukucitira coipa, ine osakuululira, ndi kukucotsa kuti upite mumtendere; ndipo Yehova akhale nawe, monga anakhala naye atate wanga.

14. Ndipo undionetsere cifundo ca Yehova, si pokhala ine ndi moyo pokha, kuti ndingafe;

15. komanso usaleke kucitira cifundo a m'nyumba yanga nthawi zonse; mungakhale m'tsogolomo Yehova atathera adani onse a Da vide pa dziko lapansi.

16. Comweco Jonatani anapangana pangano ndi nyumba ya Davide, ndipo Yehova anakwaniritsa izi polanga adani a Davide.

17. Ndipo Jonatani anamlumbiritsa Davide kaciwiri, cifukwa anamkonda; popeza anamkonda monga anakonda moyo wa iye yekha.

18. Tsono Jonatani ananena kwa Davide, Mawa mwezi ukhala; ndipo adzakufuna, popeza udzasoweka pamalo pako.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 20