Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 14:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo kunali m'mene Sauli anali cilankhulire ndi wansembeyo, phokoso la m'cigono ca Afilisti linacitikabe, nilikula; ndipo Sauli ananena ndi wansembeyo, Bweza dzanja lako.

20. Ndipo Sauli ndi anthu onse amene anali naye anaunjikana pamodzi, naturukira kunkhondoko; ndipo taonani, munthu yense anakantha mnzace ndi lupanga, ndipo panali kusokonezeka kwakukuru.

21. Ndiponso Ahebri akukhala nao Afilisti kale, amene anaturuka m'dziko lozungulira kukaiowa nao kuzithando; iwonso anatembenukira kuti akakhale ndi Aisrayeli amene anali ndi Sauli ndi Jonatani.

22. Anateronso Aisrayeli onse akubisala m'phiri la Efraimu, pakumva kuti Afilisti anathawa, iwo anawapitikitsa kolimba kunkhondoko.

23. Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lija; ndipo nkhondo inapitirira pa Betaveni.

24. Ndipo Aisrayeli anasauka tsiku lija; pakuti Sauli anawalumbirira, kuti, Atembereredwe iye wakudya kanthu kufikira madzulo, ndikabwezere cilango adani anga. Motero anthu onse anakhala opanda kudya.

25. Ndipo anthu onsewo analowa munkhalango, panali uci pansi.

26. Ndipo pakufika anthuwo m'nkhalangomo, onani, madzi a uci anacuruka; koma panalibe munthu mmodzi anaika dzanja lace pakamwa, pakuti anthuwo anaopa tembererolo.

27. Koma Jonatani sanamva m'mene atate wace analumbirira anthu; cifukwa cace iye ana tam balitsa ndodo ya m'dzanja lace, naitosa m'cisa ca uci, naika dzanja lace pakamwa pace; ndipo m'maso mwace munayera.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 14