Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 22:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo mfumu ya Israyeli ananena ndi anyamata ace, nati, Kodi simudziwa kuti Ramoti Gileadi ngwathu, ndipo tangokhala cete, osaulanditsa m'dzanja la mfumu ya Aramu.

4. Tsono anati kwa Yehosafati, Kodi udzapita nane kunkhondo ku Ramoti Gileadi? Ndipo Yehosafati anati kwa mfumu ya Israyeli, M'mene ukhalira iwe ndi momwe ndikhalira ndine; anthu anga monga anthu ako, akavalo anga monga akavale ako.

5. Ndipo Yehosafati ananena ndi mfumu ya Israyeli, Fuusira ku mau a Yehova lero.

6. Pamenepo mfumu ya Israyeli inasonkhanitsa aneneri ngati anthu mazana anai, nanena nao, Kodi ndizimuka kukathira nkhondo pa Ramoti Gileadi, kapena ndileke? Nati iwo, Kweraniko; popeza Ambuye adzaupereka m'dzanja la mfumu.

7. Koma Yehosafati anati, Kodi pano palibe mneneri wina wa Yehova, kuti tifunsire kwa iye?

8. Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Alipo munthu wina kuti tifunsire kwa Yehova mwa iye; koma ndimuda, popeza samanenera za ine zabwino, koma zoipa; ndiye Mikaya mwana wace wa Yimla. Nati Yehosafati, Isamatero mfumu.

9. Tsono mfumu ya Israyeli anaitana mdindo, nati, Kamtenge msanga Mikaya mwana wa Yimla.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 22