Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 21:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anthu aja awiri oipawo analowa, nakhala pamaso pace, ndipo anthu oipawo anamcitira umboni wonama Nabotiyo, pamaso pa anthu onse, nati, Naboti anatemberera Mulungu ndi mfumu. Pamenepo anamturutsa m'mudzi, namponya miyala, namupha.

14. Pomwepo anatuma mau kwa Yezebeli, nati, Naboti waponyedwa miyala, nafa.

15. Ndipo kunali, atamva Yezebeli kuti anamponya Naboti miyala nafa, Yezebeli anati kwa Ahabu, Taukani, landirani munda wamphesa wa Naboti Myezreeli uja anakana kukugulitsani ndi ndarama, popeza, Naboti sali ndi moyo, koma wafa.

16. Ndipo kunali, atamva Ahabu kuti Naboti wafa, Ahabu anauka kukatsikira ku munda wamphesa wa Naboti, kuulandira.

17. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Eliya waku Tisibe, nati,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 21