Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 18:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo atapita masiku ambiri, mau a Yehova anafika kwa Eliya caka cacitatu, nati, Kadzionetse kwa Ahabu, ndipo ndidzatumiza mvula padziko.

2. Ndipo Eliya anamka kukadzionetsa kwa Ahabu. Ndipo njala inali yaikuru m'Samaria.

3. Ndipo Ahabu anaitana Obadiya woyang'anira nyumba yace. Koma Obadiya anaopa ndithu Yehova;

4. pakuti pamene Yezebeli anapulula aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri zana limodzi, nawabisa makumi asanu asanu m'phanga, nawadyetsa mkate ndi madzi.

5. Ndipo Ahabu anati kwa Obadiya, Kayendere dziko lonse ku zitsime zonse zamadzi, ndi ku mitsinje yonse, kapena tikapeza msipu ndi kusunga moyo wa akavalo ndi nyuru, zingafe nyama zonse.

6. Tsono iwo awiri anagawana dziko kukaliyendera; Ahabu anadzera njira yace yekha, ndi Obadiya njira yina yekha.

7. Ndipo Obadiya ali m'njira, taona, Eliya anakomana naye; iye namdziwa, namgwadira, nati, Ndinu kodi mbuye wanga Eliya?

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 18