Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 11:34-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Koma sindidzalanda ufumu wonse m'dzanja lace, koma ndidzamkhalitsa mfumu masiku ace onse, cifukwa ca Davide mtumiki wanga amene uja ndinamsankha, cifukwa kuti anasunga malamulo anga ndi malemba anga.

35. Koma ndidzalanda ufumu m'dzanja la mwana wace, ndi kupatsa iwe mafuko khumi amene.

36. Ndipo ndidzamninkha mwana wace pfuko limodzi, kuti Davide mtumiki wanga akhale cikhalire ndi nyali pamaso panga m'Yerusalemu, mudzi umene ndinadzisankhira kuikapo dzina langa.

37. Ndipo ndidzakutenga iwe, ndipo udzacita ufumu monga umo ukhumbira moyo wako, nudzakhala mfumu ya Israyeli.

38. Ndipo kudzakhala kuti ukadzamvera iwe zonse ndikulamulirazo, nukadzayenda m'njira zanga ndi kucita cilungamo pamaso panga, kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga anatero Davide mtumiki wanga pamenepo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndidzakumangira ndi kukukhazikitsira nyumba, monga nelinammangira Davide, ndipo ndidzakupatsa iwe Israyeli.

39. Ndipo cifukwa ca ici nelidzazunza mbumba ya Davide, koma si masiku onse ai.

40. Cifukwa cace Solomo anafuna kupha Yerobiamu, ndipo Yerobiamu anathawira ku Aigupto kwa Sisaki mfumu ya Aigupto, nakhala m'Aigupto kufikira imfa ya Solomo.

41. Ndipo macitidwe otsiriza a Solomo, ndi nchito zace zonse anazicita, ndi nzeru zace, kodi sizilembedwa zimenezo m'buku la madtidwe a Solomo?

42. Ndipo masiku amene Solomo anakhala mfumu ya Aisrayeli onse m'Yerusalemu anali zaka makumi anai.

43. Ndipo Solomo anagona ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide atate wace; ndipo Rehabiamu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 11