Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 10:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo mfumu Solomo ananinkha mfumu yaikazi ya ku Seba cifuniro cace conse anacipempha iye, osawerenga cimene Solomo anamninkha mwa ufulu waceo Momwemo iye anabwerera namukanso ku dziko lace, iyeyo ndi anyamata ace.

14. Tsono kulemera kwace kwa golidi anafika kwa Solomo caka cimodzi kunali matalenti mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi liimodzi a golidi,

15. osawerenganso winayo wa anthu a malonda oyendayenda, ndi wa amalonda ena, ndi wa mafumu onse a Arabu, ndi wa akazembe onse a madera.

16. Ndipo mfumu Solomo anapanga zikopa mazana awiri zagolidi wonsansantha, cikopa cimodzi cinapangidwa ndi masekeli mazana asanu ndi limodzi.

17. Ndi malihawo mazana atatu a golidi wonsansantha, libawo limodzi linapangidwa ndi miyeso itatu ya golidi; ndipo mfumu inazisungira zonse m'nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano.

18. Ndipo mfumu inapanga mpando waukulu wacifumu waminyanga, naukuta ndi golidi woyengetsa.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 10