Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:21-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo pamene panafika tsiku loyenera, tsiku la kubadwa kwace kwa Herode, iye anawakonzera phwando akuru ace ndi akazembe ace ndi anthu omveka a ku Galileya;

22. ndipo pamene mwana wamkazi wa Herodiya analowa yekha nabvina, anakondwetsa Herode ndi iwo akukhala naye pacakudya; ndipo mfumuyo inati kwa buthulo, Tapempha kwa ine ciri conse ucifuna, ndidzakupatsa iwe.

23. Ndipo anamlumbirira iye, kuti, Ciri conse ukandipempha ndidzakupatsa, kungakhale kukugawira ufumu wanga.

24. Ndipo anaturuka, nati kwa amace, Ndidzapempha ciani? Ndipo iyel anati, Mutu wace wa Yohane Mbatizi.

25. Ndipo pomwepo analowa m'mangu m'mangu kwa mfumu, napempha kuti, Ndifuna kuti mundipatse tsopano apa, mutu wace wa Yohane Mbatizi mumbizi.

26. Ndipo mfumu inamva cisoni cacikuru; koma cifukwa ca malumbiro ace, ndi ca iwo akukhala pacakudya, sanafuna kumkaniza.

27. Ndipo pomwepo mfumu inatuma mnyamata, namlamulira akatenge mutu wace; ndipo iye anamuka namdula mutu m'nyumba yandende;

28. natengera mutu wace mumbizi, naupereka kwa buthulo; ndipo buthu linaupereka kwa amace.

29. Ndipo m'mene ophunzira ace anamva, anadza nanyamula mtembo wace nauika m'manda.

30. Ndipo atumwi anasonkhana kwa Yesu; namuuza ziri zonse adazicita, ndi zonse adaziphunzitsa,

31. Ndipo Iye ananena nao, Idzani inu nokha padera ku malo acipululu, mupumule kamphindi, Pakuti akudza ndi akucoka anali piringu piringu, ndipo analibe nthawi yokwanira kudya.

32. Ndipo anacokera m'ngalawa kunka ku malo acipululu padera.

33. Ndipo anthu anawaona alikumuka, ndipo ambiri anawazindikila, nathamangira limodzi kumeneko pamtunda, ocokera m'midzi monse, nawapitirira.

Werengani mutu wathunthu Marko 6